Mtsogoleri wa chipani cha DPP a Peter Mutharika wapempha anthu a m’boma la Balaka kuzavotela chipanichi ngati akufuna chitukuko.
A Mutharika ati iwo adzapitiliza zitukuko zonse zimene anaziyamba.
Iwo ati adzapitilizanso kupereka chakudya kwa anthu omwe pakadalipano akhudzidwa ndi njala.
A Mutharika amema anthu a m’delali kuti akhale ndi chiphaso chaunzika komanso adzalembetse mu kaundula wa oponyera voti kuti adzathe kutenga nawo gawo pa chisankhochi.