Yemwe amayankhulira mgwirizano wa Tonse, Kamuzu Chibambo wati mafuta a galimoto omwe nduna komanso alembi m’boma amalandira atsike kuchoka pa 2000 liters kufika pa mulingo osapyola 750 liters pamwezi ngati njira imodzi yotetezera chuma chadziko lino.
Chibambo, yemwenso ndi mtsogoleri wa chipani cha Peoples Transformation-PETRA walankhula izi pa msonkhano wa olemba nkhani munzinda wa Blantyre.
Read also: Breaking News: Truck carrying maize catches fire near Thabwa Roadblock in Chikwawa
Read also: President Chakwera’s austerity measures: A Case of “Do as I say, not as I do”?
Read also: UTM Spokesperson Felix Njawala Satisfied With The New Cabinet
Iye watsindika kufunika kokhazikitsa kapena kutsatira mfundo zotukulira chuma kuti dziko lino lidzitha kukhala ndi ndalama zothetsera vuto lakusowa kwa ndalama zakunja.
Atakumana atsogoleri a Tonse miyezi yapitayo, Chibambo adauza a Malawi kuti adakambirana mfundo zothetsera mavuto a chuma omwe ayala mphasa m’dziko lino pakadalipano.
Read also: Felix Njawala reflects on UTM’s origins and future at Masintha Ground Rally
Read also: Ministry of Education temporarily closes schools due to Cyclone Chido Threat
Read also: REPATRIATION OF ETHIOPIAN ILLEGAL IMMIGRANTS COMMENCES





