1001734676

Wolemba: Racheal Julaye

Anthu osadziwika akuganizilidwa kuti aba m’modzi mwa akukuakulu a kampani ya Universal Industries Muhammad Kasman lachitatu mu mzinda wa Lilongwe.

Mneneri wa polisi ya Lilongwe Hastings Chigalu watsimikiza za nkhaniyi pomwe wati Kasman yemwe ndi mzika ya Britain, wabedwa akuchokera ku mzikiti mu mzindawu.

”Pakadali pano tapeza iPhone ya a Kasman koma sititchula pomwe taipeza poti izi zitha kusokoneza kafukufuku,” watero Chigalu.

Iye wati Kasman amayendetsa galimoto la mtundu wa Toyota Fortuner CP 10842 ndipo anadabwa kuona kuti nsewu watsekedwa kutsogolo ndi anyamata omwe amaguza ngolo ndipo atatuluka kuti akaone ndi pomwe anthuwa anamugwira ndikumulowetsa m’galimoto yawo.

Chigalu wati pakadali pano kafukufuku Ali mkati kuti adziwe cholinga cha anthuwa komanso kupulumutsa bamboyu.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  Malawi's presidential puzzle: Unpacking the strengths and weaknesses of Chakwera and Mutharika

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *