IMG 20220507 WA0068

Atatopa ndikudikira kuti boma komanso andale awakonzere msewu olumikiza maboma a Dedza ndi Salima kudzera ku dera la Kasumbu, anthu okhala m’madera a Mfumu Madzumbi Nakaona, Chiwamba ,Ndembo ndi nzoola m’dela la Mfumu yayikulu Kasumbu ku Dedza akupala okha ndi makasu msewu wotalika makilomita 12 omwe ndioipa kwambiri.

A Gulupu a Madzumbi atiuza kuti anaganiza zochita izi kaamba kakuti kwanthawi yaitali akhala akuvutika kwambiri popita ku msika kukagulitsa mbewu, komanso kukapeza zofunikira pa moyo wawo watsiku ndi tsiku.

Iwo atinso chifukwa china nchakuti msewu akupalawu ndi wachidule kuyerekeza ndikuzungulira ku boma la Dedza koyenda ma ola 9.

Mafumu ndi anthu kumeneko apempha akulu akulu kuti asiye kuwakumbukira nthawi ya chisankho yokha komanso kuthana mavuto omwe akukumana nawo.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *