FB IMG 1733287665233
Listen to this article

M’mawa wa lero lamulungu pa 1 December, 2024, His Excellency Prof Arthur Peter Mutharika ndi chipani chonse cha Democratic Progressive Party ( DPP) mchigawo chakummwera chikhala chikulowera Ku chigwa cha nsinje wa Shire.

Ulendowu wakonzedwa m’cholinga chokawadziwitsa anthu za kalembera wa mavote amene alinkati m’ma boma a Nsanje ndi Chikwawa kuphatikiza ma maboma ena monga Mangochi, Lilongwe komanso Mzimba.

Akulu-akulu a Chipani cha DPP, monga Mlembi Wamkulu Olemekezeka a Peter Mukhito, wachiwiri kwa mtsogoleri mchigawo chakummwera olemekezeka a Joseph Mwanamvekha MP, Mkulu okonza misonkhano m’chipani cha DPP olemekezeka a Sameer Suleman MP, Regional Governor Olemekezeka a Charles Mchacha MP komanso aphungu ndi ma khansala mchigawochi ndi amene akuyembekezeka kukalankhula m’malo onse amene mwakonzedwa misonkhano.

See also  Former President Peter Mutharika urges Nsanje residents to register for voting

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *