Mtsogoleri wa chipani cha MCP Dr. Lazarus Chakwera wadzudzula omwe akumalowetsa imfa ya wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino wakale Dr. Saulos Chilima munkhani za ndale.
Iwo ati anthu atenge zomwe zidatuluka mulipoti la akatswiri am’dziko la Germany komanso madotolo a m’dziko muno zokhudza ngozi ya ndege yomwe idapha a Chilima ndi anthu ena 8.
Mtsogoleriyu wati iwo ndi a Chilima anagwilizana zopanga ndale zotukula miyoyo ya a Malawi osati ndale zopakana matope.
Iwo ati ndi mtsogoleri yemwe wachita zitukuko zosiyanasiyana m’dziko muno ndipo athokoza anthu achipanichi powapasanso mwayi oti apitilize kutsogolera chipanichi.
Read also: Is Israel moving its Eswatini embassy back from South Africa?
Read also: Key questions answered in Chilima plane crash inquiry
Read also: Nine Women Rise: 2025 Elections Mark Historic Shift Toward Gender-Inclusive Leadership

