Thursday, March 28
Shadow

Khoti Lati Zionetsero Za Mawa Zipitilire Ku Lilongwe

Bwalo la milandu lati ziwonetselo zomwe omenyela ofulu ena akonza mawa, Lachitatu munzinda wa Lilongwe zipitilire.

Oweruza milandu kubwalo lalikulu, Simeon Mdeza ndiye wapereka chigamulo-chi kuchotsa chiletso cha DC wa boma-li Dr. Lawford Palani.

Palani adaletsa zionetserozi ati poti apolisi atangwanika ndikupeleka chitetezo m’malo omwetsela mafuta a galimoto.

Komabe chigamulo-chi chati odandaula monga Kingsley Mpaso, bungwe la Human Rights Ambassadors, Ida Mazinga ndi Ben Longwe sakuyenela kutenga nawo mbali pa ziwonetselozi.

Izi zili chomwe-chi chifukwa choti pali mulandu wina omwe ena anakasumila anthuwa m’mwezi wa July chaka chino kuti asachititse ziwonetselo ati kaamba koti amalimbikitsa ziwawa.

Bwaloli lati m’modzi mwa odandaula yemwenso akukonza nawo zionetserozi, Redson Munlo atha kupitilira ndi zionetserozi koma awonetsetse kuti ndi za bata ndi mtendere.

Mwa zina, cholinga cha zionetserozi akuti nkufuna kuwuza President Lazarus Chakwera ndi wachiwiri wake, Dr. Saulos Chilima kuti atule pansi maudindo awo kapena kuti ayitanitse referendum ati kamba koti alephera kuyendetsa dziko lino.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

President Lazarus Chakwera has officially opened the Blantyre International Cancer Centre, The private health facility, has been constructed by the Thomson and Barbara Mpinganjira Foundation