Zotsatira Za Mphepo Ya Mkuntho Ya Freddy

Kutsatira mvula yochuluka imene inadza kamba ka Namondwe wa Freddy, nyanja ya Chilwa ku Zomba yadzadza pomwe madzi tsopano afika midzi yoyandikana ndi nyanjayi.

Malingana ndi a Fanuel Sadik, amene amakhala kuderali, madzi afika midzi yoyandikila doko la Kachulu komanso Mchenga ndipo anthu asamukira madera ena.

Khansala waderali, a Douglas January, anatsimikiza izi ndipo anati pakali pano kufika kunyanjaku pagalimoto ndikosatheka.

Zithuzi zikuonetsa momwe zinthu ziliri ku nyanjayi.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *