Zotsatira Za Mphepo Ya Mkuntho Ya Freddy

1 min read

Kutsatira mvula yochuluka imene inadza kamba ka Namondwe wa Freddy, nyanja ya Chilwa ku Zomba yadzadza pomwe madzi tsopano afika midzi yoyandikana ndi nyanjayi.

Malingana ndi a Fanuel Sadik, amene amakhala kuderali, madzi afika midzi yoyandikila doko la Kachulu komanso Mchenga ndipo anthu asamukira madera ena.

Khansala waderali, a Douglas January, anatsimikiza izi ndipo anati pakali pano kufika kunyanjaku pagalimoto ndikosatheka.

Zithuzi zikuonetsa momwe zinthu ziliri ku nyanjayi.

You May Also Like

More From Author

+ There are no comments

Add yours