Mphunzitsi wa timu ya FCB Nyasa Big Bullets wadandaula ndi kaimbilidwa komwe kadalipo masewero awo ndi timu ya Red Arrows loweruka lapitali.
Callisto Pasuwa wati ziganizo zina zomwe adachita oyimbira masewerowa ndi zomwe zidachititsa kuti timuyi igonje.
Pasuwa wapempha kuti chilungamo chidzikhalapo pa masewero ndi cholinga chakuti mpikisano udzikhala okomera matimu onse.
Elmabrouk Muhamad wa ku Libya ndi yemwe adaimbira masewero achibwereza omwe Bullets idagonja 2-0 pa bwalo la Heroes m’dziko la Zambia.
Kutsatira kugonjaku, Bullets idatuluka mpikisanowu 3-2 pa masewero awiri.
Read also: Fredokiss Finaly Charged With Fraud
Read also: Kaweche Scores 55% in Pre-Election Survey
Read also: Malawi Police Faulted For Failing To Arrest Machete Welding Men

