Timu ya Premier Bet Dedza Dynamos yalengeza zakubwereranso kuchisa kwa katswiri wa kutsogola, Promise Kamwendo, yemwe anautsa mpungwe-mpungwe pa msika ogula ndi kugulitsa osewera m’dziko muno.
Izi zikudza kutsatira chigamulo cha bungwe la Football Association of Malawi (FAM) chomwe linapereka kuti katswiriyu akuyenera kubwerera ku timuyi kamba kosatsata ndondomeko.
Kamwendo wapanga nawo zokonzekera ku timuyi pamene ikuyembekezeka kusewera ndi timu ya Creck Sporting pa bwalo la Dedza mu ligi ya TNM kumapeto a sabatayi.
Katswiriyu ali ndi zigoli zisanu ndi chimodzi mu ligi ya TNM pamasewero 13 omwe anasewera.
Read also: Anti Martha Chizuma Group Refutes Report That They Receive Donations
Read also: Stakeholders Raise Alarm As Local Drug Manufacturers Nears Collapse
Read also: Pempho kwa Atsogoleri a muslim Association ya Malawi

