Zipani zina zotsutsa boma m’dziko muno zati palibe cholepheretsa ziwonetsero zomwe akonza kuti zichitike tsiku la lero.
Izi zikudza ngakhale apolisi adati lero ali ndi ntchito zina zoti agwire kotero sapezekako ku ziwonetserozi.
Zokambirana pakati pa mbali ziwirizi zalephera kubwera ndi mfundo imodzi ndipo agwirizana kusagwirizana.
Zipanizi zomwe n’kuphatikizapo UDF, UTM, AFORD, DPP komanso EFP zati sizokhutira ndi kagwiritsidwe ntchito ka bungwe la MEC komanso NRB.
Kotero akuyembekezeka kuchititsa ziwonetsero ku Lilongwe zomwe akufuna kuti adindo ena ku MEC atule pansi maundindo awo komanso kusintha momwe ndondomeko ya kalembera wa zisankho ikuyendera.
Read also: Mzuzu Hotspots Drive Alarming HIV Transmission
Read also: Bright Moya Kamoto Calls for Support for School Fees in Facebook Post
Read also: Malawi Elections 2025: Fears of Disputed Results and Possible Public Rejection

